African Storybook
Menu
Cuti kwa Ambuya
Bether Mwale Moyo
Catherine Groenewald
CiNyanja
Udongo na Apiyo anali kunkala mu tauni na atate awo. Anali kukonda ntawi yamene masikulu anali ovala, cifukwa anali kuyenda pacuti kwa ambuya awo. Ambuya awo anali kunkala mu muzi wa pafupi na musinje waukulu.
Udongo na Apiyo anali okondwela cifukwa inali ntawi yoyenda pa cute kwa ambuya awo. Usiku analonga vyola vawo kukonzekela ulendo. Usiku uyo, ana awa, anakangiwa kugona ndipo anaceza usiku onse pazaulendo.
Kuseni seni anayambapo, ulendo woyenda kumunzi mu motoka ya atate awo. Anapitilila mapili, vinyama vamusanga ndiponso minda za masamba. Ana awa, anawelenga mamotoka munjila ndipo anayimba nyimbo.
Panapita ntawi ndipo ana awa anagona cifukwa analema.
Pamene anafika pa munzi, atate a Odongo na Apiyo ana usa ana. Ana anapeza ambuya awo aligone pa mpasa munsi mwa mutengo. Ambuya awo anali muzimai wampamvu, ndipo wokongola kwambili.
Ambuya anakondwela kwambili ndipo anavina vina, nayimba nyimbo zacisangalalo. Azukulu nawo anakondwela kwambili, ndipo anapasa ambuya awo mpaso zomwe anawabwelesela. "Yambililani kusegula yanga mpaso," anati Odongo. "Yambililani yanga," anati Apiyo.
Pomwe anasegula mpaso, Ambuya awo anawadalisa azukulu awo monga mwa mwambo.
Ndipo Odongo na Apiyo anayenda panja nayamba kupilikisa ma bulaula na mbalame.
Ana awa, anakwela mitengo ndipo anasewela na manzi.
Pamene kunafipa, ana anabwelela kunyumba mukudya cakudya ca usiku. Koma ana awa anagona akalibe kusiliza kudya.
Mumawa mwake, atate ake a Odongo na Apiyo anabwelele ku tauni. Ana anasala na ambuya awo.
Odongo na Apiyo anatandiza ambuya awo na zincito za panyumba. Ana awa anatapa manzi na kusakila nkuni. Anadoba mazila ndipo anatyola ndiyo mumunda.
Ambuya anapunzisa azukulu awo kupika nsima, nsomba, na ndiyo zina zakumunzi.
Kuseni kwina, Odongo anayenda kudyesela ng'ombe. Ng'ombe zina zinayenda mumunda mwa antu ena. Antuwa ankalipa kwambili ndipo ananena kuti azazigwila ng'ombe. Odongo ana punzila, ndipo anatayako nzelu kuti Ng'ombe zisazipanga milandu.
Siku lina ana anayenda ku musika na ambuya awo. Anayenda kukagulisa ndiyo za mumunda, shuga na sopo. Apiyo anali kukonda kuuza antu mitengo za vintu. Odongo anali kukonda kulongeza vintu vamena antu anali kugula.
Pakusila kwa siku ana anatandiza ambuya awo kuwelenga ndalama, ndipo pamozi anamwa tiyi.
Mwazizizi, masiku yonkala pa cute yanasila ndipo ana anafunika kubwelela ku tauni. Ambuya anapasa Odongo kapu ndipo anapasa Apiyo covala ca mpepo. Ambuya analonga cakudya capaulendo.
Odongo na Apiyo sibanafune kubwelela ku tauni. Ana anapempa ambuya awo kuti ayende nawo ku tauni. Koma ambuya anati "Ndine nkalamba ndipo siningankale mu tauni, koma mukabwela kuno kumuzi muzakanipeza."
Odongo na Apiyo analayilana na ambuya awo.
Pamene Odongo na Apiyo anabwelele ku sukulu, anauza anzao za umoyo wakumunzi. Anzao ena anakonda umoyo wamu tauni koma ena anakonda umoyo wakumunzi. Koma onse ana ananena kuti ambuya a Odongo na Apiyo ni abwino mutima.
You are free to download, copy, translate or adapt this story and use the illustrations as long as you attribute in the following way:
Cuti kwa Ambuya
Author - Violet Otieno
Translation - Bether Mwale Moyo
Illustration - Catherine Groenewald
Language - CiNyanja
Level - First paragraphs
© African Storybook Initiative 2015
Creative Commons: Attribution 4.0
Source www.africanstorybook.org
Menu
  • Navigate

    Navigate through the story by swiping right or left or clicking when the cursors changes to an arrow on the right or the left edge of the screen.

    Tap or click on the centre of the page to see, or remove the menu bars at the top and the bottom of the screen. You can also use the ESC key.

    You can use the slider at the bottom as a way to move quickly through the story. On a mobile device tap on the slider before you drag the slider button.

    Click or tap to return to African Storybook.

  • Share
    If you have a Twitter or Facebook account, you can share this story on your page or a page you manage. You can also copy the web link (URL) for this story.
    • Twitter
    • Facebook
    • Url
  • Rate
    Other visitors rated this story

    Tell us how much you liked the story – drag the scroller to highlight one or more stars
    • Submit
  • Comment
    Read other people’s comments on the story, or add your own.
    • Enter your comment
    • Name
    • E-mail
    • Post
  • Translations and adaptations
    • Vakansie by Ouma
      Afrikaans (Adaptation)
    • Vakansies by ouma
      Afrikaans (Translation)
    • في عطلة مع الجدة
      Arabic (Translation)
    • Mondli Ne Mbali Kɔsra Wɔn Nanabaa
      Asante Twi (Translation)
    • Mupumuno Abankaaka
      ChiTonga (Translation)
    • Ywomirok bothi Adhadha
      Dhopadhola (Translation)
    • Holidays with grandmother
      English (Original)
    • Mondli and Mbali visit grandmother
      English (Adaptation)
    • Visiting grandmother
      English (Adaptation)
    • Holidays with grandmother (Colour-in)
      English (Adaptation)
    • Rendre visite à mamie
      French (Translation)
    • Siwtaare bee maama
      Fulfulde Mbororoore (Translation)
    • Cuuti Kuli Banakulu
      IciBemba (Translation)
    • Amalanga wokuphumula nogogo
      isiNdebele (Translation)
    • ULilitha noLuniko batyelela umakhulu wabo
      isiXhosa (Translation)
    • UMondli noMbali bavakashela ugogo wabo
      isiZulu (Translation)
    • Abana mu biruhuko
      Kinyarwanda (Translation)
    • Likizo kwa Bibi
      Kiswahili (Translation)
    • Kumtembelea Bibi
      Kiswahili (Translation)
    • Meemè yee wùn à yaàyá
      Lámnsoʼ (Translation)
    • Ohuŋuumulira Ewa Nguhwa
      Lunyole (Adaptation)
    • Ohuŋumulira Ewa Nguhwa
      Lunyole (Translation)
    • Ekiwuumulo ni dhaadha omukazi
      Lusoga (Translation)
    • Okucaalira dhaadha omukazi
      Lusoga (Translation)
    • Akilakin Ata Egolitoe Esukul
      Ng’aturkana (Translation)
    • Amaulukho Wa Kukhu
      Oluwanga (Translation)
    • Re etela koko
      Sepedi (Translation)
    • Matsatsi a phomolo le nkgono
      Sesotho (South Africa) (Translation)
    • Morwesi le Pule ba etela nkoko
      Setswana (Translation)
    • Kwapumulo Ni Bokuku
      SiLozi (Translation)
    • Ngesikhatsi semaholide nagogo
      Siswati (Translation)
    • Mondli Ne Mbali N Kaa Ba Makpeem
      Talen (Translation)
    • Gui̱l Mandɔɔŋ
      Thok Nath (Nuer) (Translation)
    • Holodeyi na makhulu
      Tshivenḓa (Translation)
    • Ku endzela kokwana wa xisati hi tiholideyi
      Xitsonga (Translation)
  • Download to read
    Landscape version
  • Download to print
    Portrait (booklet) version
  • Download EPUB