Zama Niwopambana
Michael Oguttu
Vusi Malindi

M'bale wanga amacedwa kuuka.

Ine ndimaukam'mawa cifukwa ndine wopambana.

1

Nimatsegula mazenera kuti dzuwa lilowe.

2

"Iwe ndiwe nthanda yanga," amanena tero amai.

3

Ndimasamba masiku onse popanda thandizo lililonse.

4

Sindivutika kusamba madzi ozizira kapena kusambira sopo wobiriwira wochapira zovala.

5

Amai amandikumbutsa, "Osaiwala kutsuka mano."

Ndimayankha kuti, "Sicindingaiwale."

6

Pambuyo posamba, ndimapereka moni kwa agogo ndi amayi aang'ono.

7

Ndipo ndimavala zovala.

Ndimanena kuti, "Ndine wamkulu tsopano amayi."

8

Ndimakwanitsa kumanga mabatani ndiponso kumanga nthambo za nsapato zanga.

9

Ndimatsimikiza kuti m'bale wanga adziwa nkhani zonse za kusukulu.

10

M'kalasi ndimacita bwino m'njira iliyonse.

11

Nimacita zonse izi zabwino masiku onse.

Koma camene nikondesesa kwambili nikusowela, kuswowela ndi kusowela!

12
You are free to download, copy, translate or adapt this story and use the illustrations as long as you attribute in the following way:
Zama Niwopambana
Author - Michael Oguttu
Adaptation - Bether Mwale-Moyo, Moffat Moyo
Illustration - Vusi Malindi
Language - CiNyanja
Level - First sentences