M’ngono wanga amacedwa
kugona.
Ndimauka m’mamawa cifukwa
ndine wa ngwilo!
Ndine ndimatsegulako kuti
dzuwa lilowe.
‘‘Ndiwe nthanda yanga,’’ amatelo amai kundiwuza.
Ndimadzisamba ndekha matsiku
onse, sindifunanso thandidzo ai.
Sindimaganiza zakuti madzi
ndiyodzidzila, kapena sopo wa kamtambo
wocapila dzobvala.
Amai amandikumbutsa kuti
“osayiwala kutsuka mano”.
Ndimawayanka kuti “ine
ai, sindingaiwale ai!”
Ndikamalidza kusamba, ndimapatsa
moni agogo amuna ndi alongo
awo atate anga.
Ndimawafunila tsiku labwino.
Ndipo ndimabvala ndekha.
‘‘Ndine wamkulu tsopano amama,’’ ndimawaudza.
Ndimanga mabatani komanso
nthambo za nsapato ndekha.
Ndimayesetsa kuti mbale wanga adziwe nkhani zonse za kusukulu.
Ndimacita zonse zothekela
munjira mukalasi.
Ndimacita zabwino zonsezi
tsiku ndi tsiku.
Koma
ndimakondetsetsa kusowela
kwambili!