Awa ndi aphunzitsi anga.
Dzina lawo ndi a Akinyi.
Amatikonda kwambiri.
Aphunzitsi a Akinyi amatiphunzitsa mndandanda wa zilembo.
Amatiphunzitsa zilembo za liwu.
Nditha kutchula zilembo izi a, e, i, o, u.
Aphunzitsi a Akinyi amatiphunzitsa mitundu.
Ndimadziwa mtundu wofiira, wabuluu, wagirini, wayelo, ndi wakuda.
Nthawi yopumula timagona, aphunzitsi a Akinyi amatiimbira nyimbo kuti tigone.
Amatiimbira kanyimbo kogonetsera ana.
Nyimboyo imati:
Goonaa mwaanaa, goonaa mwaanaa.
Uleke kuliraa, uleke kuliraa.
Mbalame zonse zagona mu zisa zawo zazing'ono. Goonaa mwaanaa, goona mwaanaa.
Aphunzitsi a Akinyi amadziwa nyimbo zambiri.
Amatikambira nkhani yatsopano tsiku lililonse.
Lolemba, amatikambira nkhani zokhudza abambo amene anachita zazikulu.
Lachiwiri, amatikambira nkhani zokhudza amayi amene anachita zazikulu.
Lachitatu, amatikambira nkhani zokhudza mtengatenga ndi mtokoma.
Lachinayi, amatikambira nkhani za ulimi.
Lachisanu, timanena nkhani zathu.
Aphunzitsi athu ndi opambana ena onse pa dziko.
Ndikadzakula, ndifuna kudzakhala ngati aphunzitsi a Akinyi.