MPIKISANO WA KALULU NDI FULU
Daniel PJ Mwale and Impact Network

"Bwanji?" Kalulu anapatsa moni fulu. Kalulu anauza Fulu kuti acite mpikisano othamanga ndipo iye anavomera. Iwo anasankha bulu kuti akhale ogwira nthambo.

1

M'mamawa kutacha anayamba mpikisano wao ndipo bulu anagwira ndembera kuyambitsa mpikisano.

2

Pomwe bulu analiza wezulo Kalulu anathamanga kwambiri kusiya Fulu.

3

Kalulu podziwa kuti fulu wakhalira, anapumula pa mtengo ndipo pamenepo tulo tunamugwira nagona. Fulu atafika pamenepo anaona kuti Kalulu wagona ndipo iye anapitiriza ulendo.

4

Pomwe kalulu anauka anaona mapazi a Fulu kuti wapita kale. Kalulu anathamanga kwambiri koma sanamupeze fulu ai.

5

Kalulu anapeza kuti fulu adutsa panthambo pothera. Kalulu analuza mpikisano othamanga.

6
You are free to download, copy, translate or adapt this story and use the illustrations as long as you attribute in the following way:
MPIKISANO WA KALULU NDI FULU
Author - Daniel PJ Mwale and Impact Network
Illustration -
Language - CiNyanja
Level - First paragraphs